Friday, February 20, 2015

21 FEBRUARY: TSIKU LOKUMBUKIRA ZIYANKHULO ZATHU PADZIKO LONSE

Alick Kadango Bwanali Zomba

Chiyankhulo ndi chimodzi mwa zinthu zimene zimapereka chizindikiro kwa anthu ngati mtundu. Mtundu uliwonse umadziwika ndi chiyankhulo kapena ziyankhulo zawo powonjezera pa zinthu zina monga zizolowezi ndi makhalidwe. Chiyankhulo ndi njira imodzi imene timaonetseranso zikhalidwe zathu. Motero kuti popanda chiyankhulo ndikovuta kuti mtundu wa anthu udziwike bwinobwino. Padziko lonse lapansi pali ziyankhulo pafupifupi 7,106 malinga ndi kafukufuku wa bungwe la Ethnologue. Ku Africa kuno tili ndi ziyankhulo zambiri ndipo sichachilendo kuti dera limodzi likhale ndi ziyankhulo zingapo. Uku ndi kudala kwakukulu kwa Africa ndipo tiyenera kukhala onyadira kuti tili ndi ziyankhulo zankhaninkhani. Ku Malawi kokha kuno tili ndi ziyankhulo pafupifupi khumi ndi zisanu ndi chimodzi (16). Koma kungokhala ndi ziyankhulo zochuluka sikokwanira. Funso ndi lakuti kodi ziyankhulozi zikugwira ntchito yanji pa chitukuko cha moyo wanu, dera lanu komanso dziko lathu lino.

Ziyankhulo zosiyanasiyana zimagwira ntchito zosiyanasiyana m’dziko. Zina zimagwiritsidwa ntchito m’sukulu, zina m’maofesi, zina m’mabwalo a milandu ndi malo ena ambiri. Koma kodi udindo wosankha chiyankhulo/ziyankhulo zimene tizigwiritsa ntchito m’magawo osiyanasiyana ndi wa yani? Kodi malamulo oyendetsera dziko amanena chiyani pa za ufulu wa ziyankhulo? Malamulo a dziko lino mu Gawo IV ndime 26 amamena kuti “munthu aliyense ali ndi ufulu wogwiritsa ntchito chiyankhulo chimene akufuna….” Kodi ufulu umenewu anthu wamba timaudziwa? Ngati timaudziwa, timaugwiritsa ntchito? Ngati sitiugwiritsa ntchito, ndi chifukwa chiyani? Kodi chiyankhulo chathu chikutengapo gawo lanji pa moyo wathu, pa chitukuko cha dera lathu komanso dziko lathu? Kodi tikukhutira ndi momwe ziyankhulo zathu zikugwirira ntchito?

21 February ndi tsiku lokumbukira ziyankhulo zamakolo padziko lonse lapansi. Cholinga cha tsikuli ndi chakuti anthu komanso mayiko azitha kuzindikira ndi kulingalira bwino za ubwino kapena phindu lokhala ndi zikhalidwe komanso ziyankhulo zosiyanasiyana. Dziko la Malawi monganso mayiko ambiri mu Africa muno komanso padziko lonse, lili ndi anthu a mitundu yosiyanasiyana amene ali ndi zikhalidwe komanso ziyankhulo zosiyanasiyana. Ichi ndi chinthu chabwino chomwe tiyenera kuchinyandira kwambiri. Koma timaona kuti pazifukwa zosiyanasiyana maboma ena monga boma la Malawi amangosankha chiyankhulo chimodzi kapena zingapo kuti ndizo zizigwiritsidwa ntchito m'sukulu kapena pantchito zina zaboma. Kawirikawiri china mwa ziyankhulozi chimakhala chakunja monga Chingelezi. Zoterezi zimachititsa kuti ziyankhulo zathu zina zimene sizinasankhidwe zizioneka ngati zopanda ntchito ndipo anthu amene amaziyankhula salabadiridwa n’komwe. Choncho, kumakhala kovuta kwa anthu oyankhula ziyankhulozi kuti azitha kuchita nawo zinthu zothandiza kukweza miyoyo yawo kapena dziko lawo monga pa maphunziro chifukwa alibe njira yoperekera maganizo awo. Kugwiritsa ntchito chiyankhulo chakunja sikolakwika koma monga malamulo akunenera, ziyankhulo zathu zizipatsidwanso danga lokwanira.

Kodi tsiku la 21 February linakhazikitsidwa bwanji? M'chaka cha 1952 m'dziko lomwe lero lili Bangladesh koma panthawiyo linali gawo la dziko la Pakstani ophunzira a m'sukulu zosiyanasiyana makamakama mayunivesite anachita zionetsero zofuna kuwumiriza boma kuti lilole kuti chiyankhulo cha Bengali chipatsidwe mwayi wogwiritsidwa ntchito m'sukulu. Panthawiyo n’kuti boma litagamula kuti chiyankhulo cha Urdu ndicho chikhale chiyankhulo cha fuko. Izi zinakwiyitsa anthu ambiri amene ankayankhula chiyankhulo cha Bengali. Pazionetsero zokwiya ndi maganizowa ophunzira angapo a ku yunivesite ya Dhaka anaphedwa pamene anali kulimbana ndi apolisi pabwalo la milandu la mu mzinda wa Dhaka. Kuphedwa kwa ophunzirawa kukungotsimikizira za kufunika kolemekeza ziyankhulo zathu ndipo kuti munthu aliyense ali ndi ufulu woonetsatsa kuti chiyankhulo chake sichikuponderezedwa ngakhale chitakhala kuti anthu amene amachiyankhula ndi ochepa mwa mtundu wanji.

Pozindikira za kufunika kwa ziyankhulo zathu, m'chaka cha 1999 bungwe la UNESCO linakhazikitsa tsiku la 21 February kuti likhale lokumbukira ziyankhulo zamakolo padziko lonse. Powonjezera apo, m'chaka cha 2009 bungwe la mgwirizano wa mayiko onse la United Nations linapempha mayiko kuti ayesetse kulimbikitsa ndi kuteteza ziyankhulo zonse zimene zimagwiritsidwa ntchito ndi anthu. Bungweli linachita izi pofuna kugwirizana ndi zija anachita ophunzira a ku Bangladesh m'chaka cha 1952. Choncho, chaka ndi chaka mayiko komanso mabungwe okhudzidwa ndi maphunziro komanso chikhalidwe amakonza zochitikachitika pofuna kulimbikitsa ziyankhulo zathu. Zina mwa zochitikazi zimakhala zionetsero zosonyeza zikhalidwe komanso ziyankhulo zosiyanasiyana zimene zikupezeka m'mayiko kapena m'madera a dziko lonse lapansi.

Tsikuli likuyenera kutikumbutsa ife Amalawi za ziyankhulo zathu ndikuti tiyenera kuchitapo kanthu pothandiza kuti ziyankhulozi zisafe komanso kuti tizizigwiritsa ntchito m'sukulu komanso m'ntchito zina zambiri. Udindo wowonetsetsa kuti ziyankhulo zathu zikupatsidwa danga pa chitukuko cha dziko lino uli m'manja mwa eni ake chiyankhulo. Ngati sitichitapo kanthu ziyankhulo zathu zidzafa ndipo chikhalidwe chathu chidzafanso. Tisalole kuti ziyankhulo zathu ziponderezedwe ayi. Tikayamba ife kunyadira ndi kugwiritsa ntchito chiyankhulo chathu ena adzazindikira kufunika kwa chiyankhulocho ndikuchitenga ngati chiyankhulo china chilichonse. Tikumbukire kuti palibe chiyankhulo choposa chinzake.

Dziko la South Africa linakhazikitsa ziyankhulo khumi ndi chimodzi (11) ngati ziyankhulo za fuko ndi cholinga chofuna kulimbikitsa umodzi pakati pa nzika za dzikoli. M’chaka cha 2013, yunivesite ya KwaZulu-Natal ku South Africa konko inalamula kuti kuyambira chaka cha 2014 ophunzira ONSE a m’chaka choyamba pa yunivesiteyi aziphunzira chiyankhulo cha isiZulu ndi cholinga chofuna kumanga mtundu komano kutukula ziyankhulo zonse zam’dzikoli. Kodi zimenezi zingachitike ku Malawi kuno? Ophunzira a ku yunivesite angalole kuphunzira Cisena kapena Kyangonde? Mayiko ambiri a ku Ulaya ali ndi ziyankhulo zawozawo zimene amagwiritsa ntchito m’sukulu, m’mafakitale ndi ntchito zina zosiyanasiyana. Angelezi ali ndi chawo Chingelezi, Afalansa ali ndi chawo Chifalansa, Majelemani ali ndi chawo Chijelemani, ku Netherlands kuli Chidatchi, ku Japan ali ndi chawonso. Ku Malawi kuno tinasankha Chingelezi cha Angelezi ndi Chichewa pang’ono kuti ndizo tizigwiritsa ntchito pa ntchito zaboma. 21 February izitikumbutsa kuti Ciyawo, Citumbuka, Ellomwe, Cisena, Citonga, Kyangonde Cindali, Cisukwa, Cilambya, Cimambwe, Cinyakyusa, Cinyiha, Chichewa, Cingoni, Cinamwanga, Cisenga ndi ziyankhulo zina zonse zimene zikupezeka m'dziko muno nazo ndi zofunikira ndipo tsiku lina ngati eni akefe titachitapo kanthu zingathe kudzaphunzitsidwa m'sukulu zathu. Udindo ndi wathu, Amalawi. Ndi Ufulu wathunso.

Friday, April 4, 2014

Mikatoni: Mnzanga Wakalekale

Ine paja ndinafotokoza kale kuti kwathu n'ko Mbuna. Chinthu chimodzi chimene chimandipukwitsa kwathu kapena kuti ndizikonda ndikunyadira kwathu ndi anzanga ndi abale amene ndinakula ndi kusewera nawo limodzi.Ngakhale kuti chaka chimene ndinakhalako kwathu ndili wamkulu ndi wozindikira ndi pamene ndinali ndi zaka 12 zakubadwa ndipo ndipahunzirako sukulu materemu awiri, ndili ndi anzanga ambiri amene ndimawakumbukira mpaka lero. Ena a m'mudzi wathu komanso a midzi ina makamaka amene ndinadziwana nawo ku sukulu kwa Kaundama. Miston Chambadzana ndi mnzanga wakalekale. Iyeyu ngakhale sindinauzidwe kuti pali ubale wanji ndi ine koma ndimadxiwa kuti ndi mbale wanga ndithu chifukwa nyumba yawo inali kuseli kwa nyumba yathu panthawi imeneyo ndipo ife timadziwa kuti anthu onse a mudzi umodzi ndi pachibale. Amayi ake a Mistoni anamwalira iye ali wamngóno kwambiri ndipo enafe sitinawaone kapena kuwadziwa. Malinga ndi mwambo wa chikamwini, chifukwa chakuti bambo a Mistoni sanali a m'mudzimo atamwalira amayi ake iwo anachoka kubwerera kwawo. Choncho Mistoni anakula ngati mwana wamasiye ngakhale kuti bambo ake analipo. Mistoni anakula ndi achemwali ake akulu. Koma mwatsoka anamwaliranso mwadzidzidzi Mistoni ali wachichepere. Akuluakulu akamati umphawi siupha, ndimakhulupirira popeza ndinaonera Mistoni. Ndipo moyo wa Mistoni umandizizitswa kwambiri ndikumasinkhasinkha kuti kodi nçhifukwa chiyani Namalenga amalola kuti anthu ena azivutika moyo wawo onse pamene ena akukhala mu ulemerero. Chimene chimandisangalatsa ndiponso chimene ndimaphunzirapo kuchokera kwa moyo wa Mistoni ndi kusadandaula ndi mavuto. Masiku ano timamva za anthu akulowa m'mavuto ena aakulu monga lkulowerera chifukwa cha umphawi. Ena amalorera kuchotsa moyo wawo chifukwa cha mavuto. Koma Mistoni snalabadire za mavuto ake ndipo anali munthu wachimwemwe tsiku lililonse. Akadzuka sanali kudziwa kuti kodi tsikulo adya chani kapena avala chani. Mistoni ankadya chililichonse. ndikuti chilichonse chimene wachipeza. Komatu sanali wa misala. Mutamuona Mistoni akudya kamphiripiri wamuwisi wodzadza chikhato chake simukanaona kawiri. Koma tsabola anali chakudya cha Mistoni. Mistoni akalawa nsima anali deya wopemphetsa m'makomo mwa anthu kapena kudyana nawo kwa amene amuyitanira. Mistoni ndiye anali mnzanga wosewera naye mpira komanso phada. pakhomo pawo panali njira komanso bwalo lomwe ana ambiri tinkasewerapo. Nthawi yovuta kwambiri imene inkamusautsa Mistoni chifukwa cha mnyozo wa anzakefe inali yosewera mpira. Tikakhalapo ana ambiri ofukwa kusewera chikumasi (chikulunga) tinkagawa matimu awiri. Kuti tithe kuzindikirana tinkagwirizana kuti timu ina ivule malaya. Amene anali timu ya Mistoni ankalimbikira kuti iwo ndi amene avule malaya. Mistoni sankakhala ndi zovala nthawi zambiri makamaka malaya. Ankangoyenda mimba pamtunda. Nthawi zina ankakoleka kansalu ka kolala ndi momangamo mabatani kamene kanali ngati kotsalora malaya onse atatha. Sindidziwa ngati pogona ankavula koma tsiku lililonse amapezeka nako mkhosi. Ikafika nthawi yampira tinkamuvulitsa kuti tizitha kumuzindikira. Chinali chipongwe chabe ndipo ambuye azitikhululukira. Komatu Mistoni sankatekeseka nazo, iye kwakwe kunali kumwetulira ndipo ankachotsa ndikukayika potero, mpira ukatha nkukavalanso. Masiku nkumapita. Masiku amenewo a mishoni ankathandizako ana amasiye ndi zovala. Kawirikawiiri Mistoni ankalandra jekete lalikulu. Ndiye lomwelo limakhala gombeza lomwelo malaya. Tikamasewera mpira ngati ali mu timu yavala malaya ndiye kuti Mistoni ankasewera ali ndi jekete m'thupi. Koma monga ndafotokozera zimenezi sizinkamukhudza Mistoni. Tinkatha kulisintha dzina lake kukhala Mikatoni kapena Mikabodo koma iye sankalabada. Mistoni anayamba sukulu ngakhale sanapite nayo patali. Koma anadziwa kulemba ndi kuwerenga motero kuti anachitanso maphunziro a Sunday school ndi kalasi nabatizidwa. Ndimahulupirira kuti chinthu chinyaditsa kwambiri m'moyo mwake chinali kumangitsa ukwati woyerea. Kwathu masiku amenewo ukwatitsa ukwati wa pa mpingo chinali chinthu chamtengo wapatali. Anyamata ambiri ankalolera kupita ku maesiteti ku Kasungu kwa a Khondowe kuti akapeze ndalama yodzachitsira ukwati. Ndipo Mistoni anachita chimodzimodzi mpaka anakwatitsa ukwati wake ku Nkhoma madyerero anachitikira kwawo kwa mkazi m'mudzi mo Mphonde. Posachedwapa nditakumana naye anandiuza kuti ukwatiwu unatha moti anali kuwunguza kamsoti kena koti atenge chifukwa akuvutika kukhala yekha. Ine ndi Mistoni timacheza ndithu. Ngakhale kuti umphawi sunamuchokee kwenikweni Mistoni amadziwabe kuti ine ndi mnzake wakalekale. Akangomva kuti ndabwera amathamanga kuti mwina apeze ya sopo. Chinthu chimene chimandisangalatsa ndi chakuti sanatengeke ndi khalidwe lomwa mowa kapena kusuta fodya. Mistoni amapempherabe mpaka pano ndipo anandiuza kuti ndi mtsogoleri. Koma chisamaliro chapathupi ndiye chimamuvutirapo moti tikakumana chokhacho ndi chimene chimasonyeza kusiyana kwathu. Koma Mikatoni ndi mnzanga ndithu wakalekale!

Kwathu

Muno m'tawuni timangowonana. Anthufe tonse tli n'kwathu. Ena kwawo n'kumagomo, ena kwawo n'kunyanja, ena kwawo n'kuthegere, ena kwawo n'kuntherero kwa jiko, ena kwawo n'kumusha, ena kwawo n'kuthoni. Nthawi zina kwawo kwa munthu kumapanga munthu kuti akhale momwe alili. N'chifukwa chake nthawi zina ukadabwa ndi momwe akuchitira zinthu kapena momwe munthu wina akuyankhulira timafunsa ndithu kuti kwanu n'ku? Nanga inu kwanu n'ku. Ine kwathu n'kumsewu, ko Mbuna. Nkhani ya kwanu pena pake imakhala yovuta pa zifukwa zosiyanasiyana. Anthu amasintha kwawo pa zifukwa zosiyanasiyana: kusamuka, maphunziro, ntchito, ndale, malonda, banja ndi zina zambiri. Ife zonsezo tadutsamo koma kwathu sikunasinthe. Kwathu n'ko Mbuna. ndipotu kwanu ndi kwanu, ngakhale kutaoneka kosasangalatsa m'maso mwa anthu ena, kwanu ndi kwanu basi. Ine kwathu n'ko Mbuna, ku Mpenu ko Mazengera ku Nkhoma. Mudzi wathu uli m'mphepete mwa msewu waukulu wochokera ku Lilongwe kupita ku Blantyre pa mtunda wa makilomita 40 kapena mamayilosi 25 kuchokera mumzinda wa Lilongwe. Mudzi wathu wayandikana ndi midzi ina monga Bokonera, Mng'ona ndi Mdzinga. Kukhala pafupi ndi msewu waukuluwu ndi chinthu chimodzi china chimene timachinyadira kwambiri pa zifukwa zambiri. Mwachitsanzo, mayendedwe sizovuta. Kungokhala m'mbali mwamsewu nthawi ina iliyonse upeza galimoto yokwera kupita komwe ukufuna. Kulibe kabaza kwathu! Chokhacho ndimachinyadira kwambiri. Tikafuna kukamba za malonda a mumsewu ndiye pali nkhani koma siyabwalo lino! Mwina ena n'kumangomangonena za kwawo chikhalilenicho kwawoko sanakhaleko. Ife kwathu tinakhalako ndipo tikukudziwa bwino. Ine kwathu ndinakhalako ndithu ndipo ndimapitako zedi. Pa ubwana wanga ndinakhalako pamene ndinaphunzira sukulu, sitanadede 1 kenako pamene ndinali sitandede 5. Sitandede 1 ndinaphunzira pa sukulu ya Kaundama yomwe masiku a m'mbuyomo makamaka cha m'ma 1980 inali yotchuka kwambiri ndikusankhitsa ana opita ku ku sekondale. ndi zinthu zochepa zimene ndimazikumbukira pamene ndinali mu Sitandede 1 chifukwa mwina ndinali wachichepere. Koma pamene ndinabwereranso kumudzi kukaphunzira Sitandede 5 pali zinthu zambiri zimene zinakhazikika m'mutumu. Zina ndi monga anzanga amene ndinkasewera nawo kunyumba komanso kusukulu, zakudya ntchito komanso zosangulutsa zina monga zilombo! hahahahahaha! Pali anzanga ambiri amene ndinadziwana nawo nthawi imeneyo amene ngakhale pano timacheza kwambiri. Mnzanga woyamba ndi malemu Tenderetu (Sosten)... mzimu wake uziusa mumtendere. Za iyeyu ndinalemba kale. Tenderetu anali msuwani wanga amene anandilandira nditangofika kumudzi. Kuchokera tsiku limenelo tinkayenda ngati inswa. Ndidzamukumbukira mpaka kale Tenderetu! Amayi anga ndi Omama (mukafika kwathu adzakuwuzani kuti Omama ndani. Olipo omodzi basi). M'bele mwawo anabadwa ana asanu, amuna atatu, akazi awiri (Omama ndi Omayi). Panopa amayi anga amakhala ku Mchinji pa Boma m'mudzi mwa Robert. Koma ngakhale makolo anasamukira ku Mchinji mçhaka cha 1995, kwathu ndi ko Mbuna ndithu. Ngakhale mudzi wathu sukuoneka kusintha kapena kutukuka, ndimanyadirabe kuti ndiko kwathu ndipo ndimakhulupirira kuti sindikadakhala momwe ndilili chipanda kubadwira ko Mbuna.Tikafika kwathu amati kwabwera Oyaliki kapena o ku Zomba. Kwathu ko Mbuna. Inu kwanu nku?

Friday, February 22, 2013

Amalume Ndakhoza

Zinthu zimasinthadi. Kale silibwerera. Kodi lero mwana akakhoza mayeso a sitandede 8 makolo amachita chiyani? Ndikudziwa kuti kholo lililonse limasangalala mwana akakhoza. Mwana wanzeru asangalatsa makolo, atero Malemba. Komatu mwina makono kukhoza mayeso opitira ku sekondale kudasuluka! Simwakalenso ayi. Mumvere ife. Kaletu kukhoza mayeso a 8 siinali nkhani ya masewera. Chinali chinthu chopambana kwambiri pamoyo wamunthu! Ku Sekondale kunali kumwambatu, kopita owerengeka okha. Ena amapita atayimba sitandede 8 ka 8 kamene ena ka 14. Ee olipo kwathu odayamba 8 ife tisanabadwe, tidayamba sukulu mpaka kukawapeza. Ndi aphunzitsi omwe kumachita kuwalemekeza powaitana, oLove, oBatison! M'dziko muno mudali masekondale ochepa kwambiri. Ma MCC anali ang'onong'ono kwambiri mwinanso osakwana 10. Anthu amachoka kummwera kukaphunzira kumpoto - ku Borero MCC kapena ku Chawa MC kwa Lobi ku Dedza kapenanso ku Bilira ku Ntcheu. Ndiye ukalakwa mayeso a 8 panali zinthu ziwiri zoyenera kuchita. Kusiya sukulu kapena kubwereza basi. Kunalibe sukulu za wanthu zangoti mbwee lerozi. Zina zophunzitsira m'chilabu! Masiku amenewo kubwereza sitandede 8 sichinali chachilendo. Ndipo tinkakhulupirira kuti palibe angakhoze mayeso chaka choyamba. Koma mwina chaka chachiwiri kapena chachitatu. Ndiye kwinako tinkangosewera dala. Tikanavutikiranji ochimwene, omalume okadali m'kalasi momwemo ndiye iwe ukawapose? Kupanda ulemutu! Ndidafotokoza kale za kwathu - mopaza momwemo. Koma lero ndifuna ndilanduleko za kumtima. Nkhani imene nthawi zina imakhetsa tsozi komanso imandipatsa phwete. Mavutowa amationetsa zambiri - zopimitsa moyowu. Ndinalemba mayeso anga a sitandede 8 kachiwiri mchaka cha 1988. Pameneo nkuti mkulu wanga ali folomu 3 ku Dzenza. Malipiro a sukulu inali nkhani yaikulu kwambiri. Ndaiwala kuti zinali ndalama zingati. Mwina K10 mwinanso osakwana. Koma wopeza K1 anali mwana wamunthu - pwepwete mponda matiki. Mchimwene wangayu ankamulipiria ndi Ochimwene - kafunseni kwathu kuti Ochimwene ndani? Olipo omodzi okha mudzi wonse. Paja ndidanena kale kuti Omayi, Omama oliponso omodzi okha. Mukawapeza! Ochimwene odali ophunzitsi o ku MCC. Pa Malawi pano mphunzitsi ndi mphunzitsi. Nthawi imeneyo Malemu mchimwene Richard analinso fomu 3 olipirianso nkukhala Ochimwene omwe aja. Ndiye ine ndikalowenso pomwepo? Koma nanga ndikadatani munthu nzeru ndili nazo! Ndinali wanzerutu ine. Mukafunse a Maliko ku Dzalanyama akakuwuzani "N'dadziwatu ine kuti m'dzadziwa; tsono m'dadziwira ku?" hahahahahaha! Ine ndidadziwadi chaka chimenecho ndipo ndidadziwira ku Mtendere, kwa Malirana. Lidali lachisanu pa 14 October 1988. Sabata yathunthu yatha chilengezereni mayeso a sitandede 8. Ife osamva kuti mayeso anayenda bwanji. Titatsakamira m'nkhalango ya Dzalanyama. Lamya kunalibe. Kukaona mayeso ndiye kuti wina apite ku tawuni (100Km). Galimoto kunalibe. Ndiye kumangodzikhalira ngati makedzana. Tsiku limeneli linatalika kwambiri. A Hedi anapeza mwayi wokwera nawo galimoto ya Folositi kupita ku tawuni kukaona mayeso. Galimoto ikapita ku tawuni inali chaka isanapotoloke. Mbuzi mukaimasula sikumbuka kubwerera m'khola. Galimoto ikapamita kutawuni masiku amenewo imadzaza - opita kuchipatala, kuchigayo, ena akalaweko kazibeki, ena wa kwawo, ena obwerera. Galimoto inali imodzi. Timadziwa kulira kwake. Tinkaizindikira ngakhale ili mitunda isanu. Nthawi inali cha m'ma 4koloko masana. Tinamva mzizima wa landrover kuti yafika ku ofesi. Kaya chinachitika ndi chiyani kuti ifike masana tsiku limenelo? Nthawi yake inali 10 koloko usiku zingavute chotani. Ine ndi mnzanga Innocent tinangodzambatuka kusiya mpira, wautali. Pakanakhala mphoto za mpikisano wothamanga tsiku limenelo tikanalandirako. Tikuti tizifika pa chipata cha ofesi, atulukira adalayivala bambo Lipenga, anzawo a bambo anga. Ndimacheza nawo kwambiri masiku ano. Munthu wopanda zibwana. Makofi saumira. "Ndiye mukuthamangira kuti ana opanda nzeru inu. Ntchito kumangosewera mpira ndikudya maula!" Anakalipa maso ali psu ndi ukali! Jega! Thukuta lonse gwa! Maso phethipethi! Nkhope zyoli -thupili silinalinso langa. ndinamuyang'ana Innocent! Anayamba kusisima! Thanthwe long'ambikatu ndibisale momwemo! Lili kuti? Lindimeze ine lero, dziko landida! "Ndikunamatu mwakhoza pitani kwa a hedi anu akakuwuzeni." Timve ziti? Mulungu aziwakhululukira ndithu! Pa 14. Pakatikati pamwezi! Osati kuti masiku ena amakhala ngati pa 27 pakhomo pathu ayi. Ife nthawi zone panali pa 14. Koma nanga pa 14 khobidi ukabwereka kwa yani? Kwada! Tinakhala pakhonde.Pa siwa. Chimwemwe chija chinali chisoni. Ngati nthanotu! Aliyense kumangosisima. Kodi ndinalakwa kukhoza mayeso. Sukulu yonse tinakhoza anthu atatu okha ine ndekha wosankhidwira ku sukulu ya National, ya Katolika! Mulungu akandikondera bwanji kuposa pamenepa? Ndinawayang'ana amama. Anali chete. Ndinadziwa chimene chinali mumtima mwawo. Mwezi umenewo ndinali nditawasungitsa K20 (ananena kuti andisungire). Koma sanasunge. Anagula chakudya inenso ndinadya nawo! Mlandu wathu. Amama anali ndi manyazi mumtima! Musadandaule amama! Komatu ine ndalamazi ndinkakonzekera kudzapitira ku sekondale chifukwa chikhulupiriro ndinali nacho ndithu. Kumene ndinazipeza ndalamazi ndi nkhani ina. Komatu ine sindinali manjalende. Ukaipa dziwa nyimbo. Ndinkapeza kangachepe kothandizira pakhomo ngakhale ndinali wamng'ono. Zikomo madala pondiphunzitsa ntchito zanu zaluso. "Komatu paja amalume ako anati ukakhoza udzapite ku Kasungu akakupatsa fizi" Anatero amayi. Koma ku Kasungu ndipita ndi miyendo. Sikolira ndalama ya basi. Madala anali phee ngati sizikuwakhudza. M'thumba mwangamu munali K8. Ingakafike ku Kasungu? Usiku umenewo amama anayenda khomo ndi khomo kusakasaka khobi, olo! Chisoni chinakula. Ndakhozeranji ine? Lachiwiri pa 18 sukulu zatsekulira. Anzathu alowa m'kalasi. Ife tikadali kosaka makobidi oyendera kupita ku Kasungu m'malo molowera mtunda wa Dedza. Mwana wamwamuna n'kabudula mbambadi. Ndi K8 yanga pathumba ndinanyamuka ku Dzalanyama pa lole yonyamula nkhuni yaulere! Pamwamba neng'a! Alemekezeke wamwambamwambayo. M'mene imati 9 koloko mnyamata wafika mu Lilongwe, K8 yake pathumba, khadi la Kongiresi mbali inayi, wa ku Kasungu. Ndinafika ku ofesi ya Khondowe pafupi ndi depoti ya basi - Khondowe wake yemweyu mukumudziwayu. Anali bwana wa amalume anga. Kumene kuja ndinafunsa ngati kunali galimoto yopita ku Esiteti imene amagwirako ntchito amalume anga. "Ayi kulibe koma ilipo ina yopita esiteti ina ku Kasungu komweko. Utha kukwera nawo ukatsikira pa Bua usanafike pa Kasungu kwinako ukakwera matola kapena basi" anatero alonda! Palibe vuto. M'mene imati 10 koloko wanyamuka mnyamata kusiyana ndi Lilongwe kuloza Kasungu. Galimoto yaulelenso iyo! M'mutumu maganizo khumi ndi asanu. Mulungu sataya wake. Khalekhaleni uyo tafika pa Bua. Akuti basi ife tikukhotera uku. Inu mupeze matola kufika paboma kwinako mukakwera basi yopita kwa Wimbe. M'mimbamu njala ndiye yayamba kuluma. Koma K8 ndikayamba kugulira nzimbe pano ndikafika nayo? Ndinalingalira amayi anga m'mbuyomu. Ndinadziwa kuti anadziona iwo olakwa pogwiritsa ntchito ndalama zimene anandisungira. Koma akanachita chiyani munthu wa mayi ana ali ndi njala. Akanasunga bwanji ndalama pakhomo palibe ufa. Amama musadandaule. Mulungu atisamalira tonse. Ali makono bwenzi nditawaimbira foni amama kuti ndili pa Bua kudikira matola, ndayenda bwino. Ha! 1988! Kwii yaima ya polisi. Landrover yakuda ija. "Ukupita kuti ayise?" Yaulelenso? Kwera, ulipira 30tambala! Dziko ili sungalimvetse. Mphindi zochepa ndafika pa Kasungu, ndatsala ndi K7.70 yanga. Wimbe via Mtunthama! Chitero chikwangwani cha bsi pa Kasungu! Ndaipeza basi ija ili khirikhirikhiri! Mwana wamunthu atakungana pa depoti ya Kasungu. Thupi lonse tsembwe. Basi ndiye ndi imeneyi, koma ndikwera? Chipwirikiti chinali pakhomo la basicho n'nali n'sanachipenyeko m'moyo wanga. Mantha anandigwira. Kodi ikandisiya basi imeneyi ndikagona kuti? Ndiyenda bwanji? Ndiwauza bwanji amama? Amalume sakudziwa kuti ndikubwera. Mwina akadadzandichingamira pa boma pano. Poyang'anitsitsa ndinaona kuti pakhomo la basi paja panali mayufi, amene anali ndi khadi ndi amene amaloledwa kulowa. Inetu monga nzika yokhulupirika khadi ndinali nalo. Ndilephereranji kukwera basi. Ndinalimba mtima. Ndafika pakhomo, K7.70 yanga m'thumba khadi langa m'manja. "Talowa iwe!" Ine selelu, dyadyamphireni! Posakhalitsa wakhulula buleki dalayivala! Wapsa wa kwa Wimbe. Khadi langa m'thumba ndalama pamanja kuti kondakitala akafika ndimve kuti ananena kuti ndalama zingati? Kaya zikwana? Zikaperewera ndidandaula. Ndimuuza kuti ndangokhoza mayeso ndikukapempha fizi ko Malume. Monga samvetsa? Mtunthama, ikadali chidzadzire basi. Dzidzidzi, Wimbe Trading Centre! Masitolo ali ndandanda. Yafika basi. Insipekitale, kondakitala sadzaoneka! Ine tsikuu, ze! Kupisa m'thumba, ilipo K7.70. Khadi mbali inayi. Ndafikatu ine kwa Wimbe. Ndalipira 50tambala kuchoka ku Dzalanyama kuja kudzafika kwa Wimbe. Kulipiranso ku galimoto ya polisi. Lili lero ndikanati ndipereka umboni pa zazikulu zomwe Mulungu anandichitira. Ku Dzalanyama kuja tinali ndi abwana a Banda amene kwawo kunali ku Kasungu ndipo ndi amene anandiuza momwe ndingayendere. Akazi awo anali aphunzitsi anga ndipo anandiuza kuti ndikafika pa Wimbe ndikapite ku sukulu komwe bambo awo a Kayembe ankaphunzitsa. Fikani kumene kuja, chisomo chokhachokha. "Ugone, Moses akabwera akuperekeza ku Kabuma mawa m'mawa sipatali." anatero mayi ake a Moses. Kwiyo yalira nkhukhu. Mwana wakhoza. Ambuye azilemekezeka ndithu. Usiku umenewo tinachezera kucheza ndi Moses. Moses anali mnzanga pamene ankakhala ndi achemwali ake ku Dzalanyama kuja koma tsopano anali kutchuthi kwa makolo ake. M'mawa tinayenda pansi mitunda ingapo kundiperekeza kwa amalume anga. Kungondiona amalume, sichimwemwe chakecho. Moyo wanga unasinthiratu. Chimvereni zotsatira za mayeso kanali koyamba kuonetsa nkhope ya chimwemwe. Chisoni chonse chinatha. Koma amama kaya anali ali bwanji? Ulendo wa ku sukulu sunalinso wachewuchewu. K300 pathumba - Leather and Luggage, gombeza, nsapato, patapata, sitonkeni. Mungawadziwe Oyaliki? Kufika kusukulu, kulipira fizi yunifolomu zonse kukwana K104. Chenji chambirimbiri! Ambuye azilemekezeka ndithu! Uwuse mu mtendere mzimu wa amalume, Harrison Bauleni Kuchiudza (HBK)!

Wednesday, February 6, 2013

Madala: Mphawi Wachimwemwe

Kodi ndi chiyani chimakupatsani chimwemwe m'moyo mwanu? Chuma? Ntchito? Mkazi? Mwamuna? Maphunziro? Nzeru? Anzanu? Chiyani? Aliyense ali ndi chinthu chake chimene chimamupatsa chimwemwe komanso chimene amadana nacho kwambiri. Ena akapata ndalama sasowa, amafuna aliyense amupatse moni ndipo adziwe kuti zinthu zikuyenda. Anthu otere akapsa m'thumba ndi nkhope yomwe imakhala ya makwingwirima. Ndalama zimabweretsa anansi. Zikatha, anansinso amathawa. Komanso nthawi zina ndalama zimabweretsa adani. Kunja kunotu kuli kaduka kapena nkhwidzi. Wina asakwete, walakwa, avala ufiti kapena umbava. "Akusolola" timatero! Moyo wa masiku ano ndi wovuta, popanda ndalama, dziko limayima, ulemu umatha. Angakulemekeze ndani ulibe makobidi? Umasanduka chitselekwete! Koma bwanji ukangosanja? "Yes wamkulu, Zoona abwana, eetu achikulire, shuwatu big" mayina mbwee chifukwa cha ndalama. Koma kodi munthu angakhale wosangalala popanda ndalama? Enafe tidakulira m'mavuto oposa a Majoti. Nkhani ya Majoti ndi yopeka koma yathu ndiyolula ndithu! Mutha kukamba za mavuto amtundu uliwonse amene munthu padziko lapansi pano amakumana nawo. Tadutsamo. Tatulukamo. Mukamationa kusalalaku sikuti tidakulira ku Nyambadwe! Ngakhale kwa Ntopwa kumene sikungayandikireko! Koma chinsinsi cha Mulungu amachidziwa ndani? Thupili sikuti ndi chambiko chalerochi. Ndilobadwa nalo. Takula nalo. M'mavuto omwewo. Koma chinthu chimodzi chimene ndidakula nacho ndicho kupeza chimwemwe m'mavuto! Simkuluwiko! Umphawi supha munthu! adatero madala! adalasa penipeni. Bwenzitu enafe titatsogola. Malemu Opapa (madala mzimu wanu uwuse mu mtendere), ndiye chitsanzo chabwino cha munthu wosangalala pamavuto, pamtendere. Simisala. Koma kusalitsanza dziko. Kwa anthu amene amatidziwa bwino kubanja kwathu, kuseka sitiumira, ndichizolowezi. Kodi ndimayesa kuseka ndiulele, sochita kugula! Ndikumbuka masiku amenewo tikukula, titadya mgawiwa wamadzulo opapa ndi omama otafatsa kutilakatulira nthano za pa ubwana wawo, za ku sukulu, za ku Joni.. ife tikuseka chikhakhali. Uku ndiko kudali kukhala kwawo, kukula kwathu. Kuseka sikunkalira ndalama. Osati kuseka kwa masiku ano kopemphera khobidi! Lero ndapukwa opapa: Richman Bwanali Kadango kwawo ku Chitundu kwa Che Tambala m'mudzi mwa a Chawala. Myawo wapaphata kukakwatira mchewa wa ko Mbuna ku Mpenu ko Mazengera ndikusiya Chisilamu n'kuyamba kudya kapado, mbewa, kupapira masese nkukathera mu Utimiki wa Dutch! Nthawi zina makolo akamapereka mayina kapena tikamadzipatsa mayina kaya chimakhala chiyani. Inetu bambo anga pobadwa anapatsidwa dzina loti Che Madayika. Koma atakula andziwika ndi dzina loti Richman! Kaya anali matemberero kaya. Anafa osauka. Koma wosangalala, wonjoya. Bambo anga atasiya sukulu anapita ku Joweni kukasewenza ku mgodi. Pobwera kumeneko ndipamene ankabwera ko Mbuna kenako nkukayamba ntchito ku Chongoni, ku nkhalango, ife nkumabadwa. M'banja mwathu tilipo ana asanu ndi anayi, onyamata osanu ndi mmodzi ndi otsikana otatu. Tonse tilipo. Anaigwiratu makolo. Koma sizinali zachibwana kusamalira mbumba yonseyi. Madala anali munthu wolimbikira ndi wogwiragwira. Kaya ntchito zinazi anazidziwa bwanji kaya? Kaya inali mphamvu ya uchawa kaya? Komatu ankatha chilichonse: kusoka, kusema, kuluka, kukhoma! Chilichonse chochita ndi manja. Mgaiwa ukapezeka magwero ake anali amenewa. Tikavala nkhani yake inali yomweyo. Luso lina tinaphunzirako - koma izi n'zatsiku lina. Analipo masiku owawitsa ndithu nthawi imeneyo. Kudikira madala kuti abweretse chimanga kapena ufa mpaka pakati pa usiku, tulo titachita chipongozi, nkhani zitatha, m'mimba mukubangula. Akafika munthu wamwamuna khosi litalowa mkati ndi chibinyira, kusaukira mbumba nkumati adandaula, ayi ndithu! Ayambepo kukuyalirani nthano za zimene waziona tsikulo, inu njala yonse kutha nkuseka! M'mawa sikuti agonereza ayi, buli wa kuntchito! Akasakenso. masiku n'kumapita, ana nkumakula. Madala anali ndi anzawo ankhaniankhani! Akakhala pagulu, kwawo kunali kuseka ndi kuseketsa. N'kuti kulibe anzawo? Sianzawo a ku Mchinji aja adakonzetsa thupi lawo kuti lisaonongeke pa 20 July paja? Sitinalandire ulemu ndi mphatso kwa anzawo chifukwa cha kucheza kwawo? "Atate wanu nanzanga zedi, timacheza zedi anga munthu ni mphwake" ankaterotu anzawo. Ukapita kukawayendera ku Mchinji uko adasamukira atapuma pantchito amakuyendetsa benchi iliyonse mumsika kukuonetsa kwa anzawo, "mwana wanga wa ku Zomba uja ndi ameneyu". Palibe chimene chinkawasangalatsa madala koposa kunyadira ana awo. Kodi sitinapeze malo chifukwa cha anzawo? Kodi lero ku Mchinji sikwathu chifukwa cha anzawo? Kodi lero kuti tipite ku Chongoni, kwa Kankhomba, kwa Chiphazi, ku Mpalale, kwa Ndemela, kwa Nthenda sakatilandira? Suja adatikankhira galimoto ulele titatitimira ku Dzalanyama kuja atangodziwa kuti uyu ndi mwana wa Angozo (mifunda ndiye inalipo yankhaninkhani koma munthu anali mchawa)? Lero ndikamaganizira za moyo wa bambo anga chimene ndimalingalira kwambiri ndikukhala wokondwa nthawi zonse mavuto angakule maka! Chachikulu bola uli ndi moyo ndipo moyo ndi waulele. Ukadakhala wogula bwenzi ife kulibe. Chimwemwe chili mumtimamu! Umphawi supha munthu. Ngati uli ndi moyo, manja ndi miyendo uli nazo yamika Namalenga, gwira ntchito upeze chakudya lero, usakwiyire ena ngati andiwo adakulodza. Usani mumtendere opapa. Munatiphunzitsa zazikulu!

Tuesday, January 8, 2013

Tachilowa nawo

Masiku atheradi kuchitseko. Anga bodza kuti tagonera. Ndife sundwe. 2012 tatseka tione kuti 2013 wafungatanji? Koma tisanathe mtunda mu 2013 tiyang'aneko kumbuyo. Chilumika chimenechi chinali ndi zake zosayiwalika. Pali zinthu zingapo zimene zidzandikumbutsa za chaka cha 2012, zabwino ndi zoipa zomwe. Paja amati zimakhala bwino kuyambira zabwino. Kabaza M'mwezi wa February ndinagula njinga yanga ku 5 Miles - AfriCycle. Ndiyamika Nijo mnyamata amene anandisankhira njinga imeneyi. Maso kunyoza. Atandilozera njinga imeneyi ndinkaona ngati wandisankhira chikhokhololo! Koma ayi ndithu Nijo anandisankhira Mlalu weniweni! Mlalu wanga wandionetsa malo m'chaka chimenechi. Mwa malo amene ndidzawakumbikire chifukwa cha mlaluwu ndi Mwandama (kuja kunakafika Mlembi wa Bungwe la Mgwirizano wa Mayiko onse a Ban Ki- Moon, ku Zomba kuno, mudzi wa Kansonga m'chigwa cha pakati pa mapiri a Zomba ndi Malosa - malo okongola kwambiri mudzi umene ukudyetsa tawuni ya Zomba ndi zipatso, komanso ku Phalombe. Mlaluwu wandionetsa Chingale, Mayaka, Ulumba ndi malo ambiri mu Zomba muno. Imfa ya Bingu 2012 chinali chaka chosautsa kudziko lathu lino. Nthawi zina ukamaona momwe atsogoleri athu amatumbwira akakhala pampando maganizo amayamba kubwera kuti mwina n'takhala ine zimenezi zingathe. Koma zikuoneka kuti aliyense akakhala pachimpando chimenechi amaona ngati iye ndiye namalenga wa tonsefe. Komatu kumwambako Chisumphi alipo ndithu ndipo dongosolo lake palibe angalimvetse ngakhale amene mukuyti ndi aneneri olulawa! Iye ndi tsidya lina. Chili kuti lero chitsulo cha njanji? Mwina chidakathera pachipala! Achinyenyanyenya? Amayi samalani. Kuno ndi kunja kudayanja lichero! Richard (uwuse mu mtendere mzimu wako) M'bele la amayi wanga munabadwa akazi awiri, Omama ndi Omayi. Mukafuna kudziwa za mayina amenewa pitani kwathu ko Mbuna mukafunse. Akakuwuzani kuti Omama ndi Omayi ndani. Richard anali womaliza kubadwa m'nyumba moMayi. Ndi ine tinangosiyana zaka zochepa kwambiri pobadwa. Tinakulira ndi kusewera limodzi makamaka pamene tonse makolo athu ankagwira ntchito ku Ngoma (Nkhalango ya Chongoni). Atatsiriza maphunziro ku Kongwe analowa ntchito ya polisi ndipo anakwera pamaudindo mpaka kufika pa Superintendent. Koma m'mwezi wa August, Richard anatisiya kuchipatala cha Nkhoma, kwathu. Komatu dzikoli ndilovutadi kulimvetsa. Zambiri ndidzakambabe koma pano tizingopemphera kuti Mulungu asamalire ana ake, Anne, King, Tiya, Shireen ndi Yankho komanso mayi awo. Yaounde Chakachi ndinachitsendera ndi ulendo wa ku Cameroon ku msonkhano wokambirana za ziyankhulo za mu Africa makamaka pa ntchito yochita kalondolondo wa chiwerengero cha ziyankhulozi, chiwerengero cha anthu oziyankhula ndi malo amene zikuyankhulidwa mu Africa muno. Unali ulendo wosangalatsa kwa ine chifukwa chakuti kanali koyamba kupita dziko limene anthu ambiri amayankhula Chifaransa mu Africa muno. Inetu Chifaransa ndinachiphunzirapo kalekale ndili mu fomu 1 ku Mtendere zaka zimenezo. Pierre et Seydou woloweza yemwe uja anatipulumutsa mpaka ife kuoneka dolo madoda oyankhula Chingerezi chokha akulephera kunena chakudya chimene akufuna kudya mu resitilanti! Sindikunena munthu ine! Koma zinali zosangalatsa kwambiri. Pamene imatha sabata ayi ndithu ife tinali titalolera Chifalansa chokwanira kufunsira (njira). 2013 wolowa chiyimirire Ngati ndikulemba lero pa 8 Januwale ndiye kuti ndalowa nawo. Koma sindinachiyambe bwino kwenikweni. Kaya ndi Namalenga kaya ndi Dyabu kaya koma ndinapezwa ndithu munthune. Pa 31 tinapita kwa anzathu kuti tikachilowere limodzi. Ndiyetu kunali kutafuna ndikukhwasula. Dansi inathyoledwa mosaona kuti apa pali mwana wanga kapena apa pali obaba ndi omama. Tangoganizani mabanja awiri ndi ana awo onse aliyense akuthyola sitepe! Panavutatu. M'mene imati 2kaloko m'mawa woyamba wa 2013 tinanyamuka wa kunyumba. Komatu chongoti lowu, pakama thasa, inu! Namo m'mimba dzambatuku! Poyerayeratu! Kuyesa kutembenukira uku, kapena uku, kapena chafufumimba, pola, nikisi! Madzi akumwa kapena? - ndiye kukolezera! Kuyesa kukanyonyomala pamtondo, kuti mwina mpweya wokha, ayi tele kuli zii! Tetetete! Kokoliko! Ukutu nkuti mnzanga wapamphasa akungouliza wa mtendere uja! Ndipite kuchipatala? Ndi adiimiti kale! Nanga zoona kuchipatalako buku tikachite kulitsekulitsa pa 1 januwale? Ndiyetu kunali gubidigubidi kuwunguza mtela. Wapezeka panadolo. Mpwintheni! Kuyesa kugona, ayi tele, tazemberatu tulo. 6 Koloko kwacha, wa kuchanjausi kukadzithira madzi kuti mwina kapena. M'mene imati 7:30 ndafika pakhomo la chipatala. Chikwangwani chikuti lero latchuthi amatsekula 8:30! Mtsonyo wakewo! Kubwerera kunyumba, mnzanga wadzuka akujijirika ndi zanyuwele! Mpamene ndimaulula kuti bwanawe mnzakone sindidatinyanthe tanyuweletu! Anangoti kukamwa yasa! Ndiyetu masana onse kunali kuliza mkonono! Koma ayi lero suyu tikupumayu! Koma wachewuchewu! Talowa ndithu ndipo tiyamika Lezayo kuti watikondera, Chichewa cha lero! Ticheza m'chaka chimenechi!

Thursday, July 19, 2012

July 20, 2011: Tsiku Losayiwalika m'Moyo Mwanga

Kulemba nkhani sichinthu chapafupi! Nthawi zina mtima umakhala ukufuna koma thupi limakhala lolefuka, nthawi imakhala yochepa, zosokoneza zimakhala zambiri. Nanji masiku ano a facebook, twitter, nyasatimes ndonzawo wokhala pansi n'kulemba nkhani kapena ndakatulo ndi munthu. ndimalakalaka ndithu nditamalemba pafupi[afupi ndipo nkhani ndi zambiri m'mutumu koma danga lochitira zimenezi ndilo lisowa ndithu. Choncho tsamba lino lakhala lili mbe chifukwa chotangwanika ndi zina ndi zina. Zina zaphindu, zina zopanda mpake pomwe. Chatsitsa dzaye ndi malingaliro amene ndakhala nawo sabata imeneyi. Kwa ine ndi onse a kubanja kwathu sabata ino chaka chatha (2011) inali nthawi yowawitsa chifukwa bambo athu anali ali m'chipatala. Mwezi wa June chaka chatha ndinapita ku Mchinji kukaona abambo anga nditamva kuti sanali kupeza bwino. Pobwerera ku Zomba chiyembekezeo ndinali nacho kuti adzapeza bwino. Patapita sabata zingapo, m'mawa wa pa 18 July ndinalandira lamya kuti madala agonekedwa m'chipatala. Mantha anandigwira chifukwa aka kanali koyamba m'moyo mwanga komanso mwa madala kugonekedwa m'chipatala. Kutacha ndinanyamuka wa ku Mchinji. Nditafika kuchipatala madala anauzidwa kuti ndafika ndipo anandiyang'ana. Ndinawayandikira kuti ndithe kuwafunsa momwe akumvera m'thupi mwawo, ndinaona pamaso pawo chilakolako chofuna kundiyankhula koma ndinadziwa kuti thupi linali lofowoka. Sindidziwa kuti madala anafuna kundiuza chiyani! Ndinawagwira dzanja koma sanasonyeze kuti ndawagwira! patapita mphindi pang'ono ndinachoka n'kukhala pambali n'kulonjerana ndi amayi komanso abambo aang'ono amene anali kudwazika matendawo. Anandipatsa uthenga wachilimbikitso koma sichinakwanire. Madala akadandiyankhula mwina ndikadalimba mtima kuti akupeza bwino. Usiku ndinapita kunyumba kukagona mtima uli wosweka ndithu. Unali usiku wautali. M'mawa kutacha pa 19 ndinapita kukawazonda. Sindinaopne kusintha kwenikweni. Mantha anandigwira ndipo ndinadziwa kuti madala sadzandiyankhulanso. Usiku wa pa 19 unandisautsa kwambiri. Sindinagone. M'mawa pa 20 July. Kutacha m'mawa ndinamva mauthenga akuti dziko la Malawi lili pamoto. Anthu anali kuchita zipolowe zosonyeza kukwiya ndi ulamuliro wa dziko lino. Mkazi wanga anali ali ku Mzuzu ndipo anandiuza kuti wakwera basi m'mawa koma akulephera kutuluka mumzindawu chifukwa cha mfuti zimene zinali kulira. Nkhawa inandigwira. Ndinamvanso kuti ku Lilongwe, ku Blantyre ndi maboma ena zinthu sizinali bwino. M'tawuni ya Mchinji munali bata ngakhale kuti m'misewu munali apolisi ochuluka kuposa nthawi zonse. 12 Koloko Masana Nthawi yowonera odwala itakwana cham'ma 12 ndinanyamuka kuti ndikazonde madala. nditatsala pang'opno ndinamva foni ya amayi kundiuza kuti ndifulumire. Mtima wanga unagunda, thupi linachite tsembwe! chongofika m'chipinda momwe munagona madala nkhope ya amayi inandiuza zonse. "Aliki bambo ako ulendo uwu"! Inali nthawi yowawitsa m'moyo mwanga! Ndinayandikira ndikuwagwedweza madala koma sanasunthe ngakhale pang'ono! Apita madala! Tsopano chaka chaka chatha. Madala anagona ku Mchinji mwakufuna kwawo. Sanafune kubwerera kwawo ku Chitundu ku Dedza. Ku Mchinji anasamukirako 1995 atapuma pantchito. Ku Mchinji kuanasanduka kumudzi kwawo, kumudzi kwathu. Anali ndi abale andi abwenzi ambiri. Onse anachitira umboni patsiku lowasunga madala pamene anafika mu unyinji wawo. Kufika kwa unyinji umenewu kunandikumbutsa ndipo kudzapitiriza kundikumbutsa moyo wa madala - kuseka ndi aliyense! Madala anali munthu wokondwa nthawi zonse ndipo ndiyamika Mulungu chifukwa cha mphatso imeneyi. Akanakhala wopanda mphatso imeneyi mwina bwenzi pano tikukamba nkhani ina. Ndi chikhumbokhumbo changa kuti ndikumbukire moyo wa bambo anga pofotokoza zina zimene zinawathandiza kukhala moyo wosangalala ngakhale atakumana ndi mavuto amtundu wanji pamoyo wawo. Tinakhalapo moyo wovutika kuthupi koma mu mtima mokha tinali anthu osangalala, achimwemwe nthawi zonse chifukwa cha madala. Mzimu wanu uziusa mumtendere Madala ndipo ngati kumene muliko ngati n'kotheka kuchita nthabwala nkumaseka, pitirizani mpaka tidzaonanenso nkusekera limodzi!