Thursday, July 19, 2012

July 20, 2011: Tsiku Losayiwalika m'Moyo Mwanga

Kulemba nkhani sichinthu chapafupi! Nthawi zina mtima umakhala ukufuna koma thupi limakhala lolefuka, nthawi imakhala yochepa, zosokoneza zimakhala zambiri. Nanji masiku ano a facebook, twitter, nyasatimes ndonzawo wokhala pansi n'kulemba nkhani kapena ndakatulo ndi munthu. ndimalakalaka ndithu nditamalemba pafupi[afupi ndipo nkhani ndi zambiri m'mutumu koma danga lochitira zimenezi ndilo lisowa ndithu. Choncho tsamba lino lakhala lili mbe chifukwa chotangwanika ndi zina ndi zina. Zina zaphindu, zina zopanda mpake pomwe. Chatsitsa dzaye ndi malingaliro amene ndakhala nawo sabata imeneyi. Kwa ine ndi onse a kubanja kwathu sabata ino chaka chatha (2011) inali nthawi yowawitsa chifukwa bambo athu anali ali m'chipatala. Mwezi wa June chaka chatha ndinapita ku Mchinji kukaona abambo anga nditamva kuti sanali kupeza bwino. Pobwerera ku Zomba chiyembekezeo ndinali nacho kuti adzapeza bwino. Patapita sabata zingapo, m'mawa wa pa 18 July ndinalandira lamya kuti madala agonekedwa m'chipatala. Mantha anandigwira chifukwa aka kanali koyamba m'moyo mwanga komanso mwa madala kugonekedwa m'chipatala. Kutacha ndinanyamuka wa ku Mchinji. Nditafika kuchipatala madala anauzidwa kuti ndafika ndipo anandiyang'ana. Ndinawayandikira kuti ndithe kuwafunsa momwe akumvera m'thupi mwawo, ndinaona pamaso pawo chilakolako chofuna kundiyankhula koma ndinadziwa kuti thupi linali lofowoka. Sindidziwa kuti madala anafuna kundiuza chiyani! Ndinawagwira dzanja koma sanasonyeze kuti ndawagwira! patapita mphindi pang'ono ndinachoka n'kukhala pambali n'kulonjerana ndi amayi komanso abambo aang'ono amene anali kudwazika matendawo. Anandipatsa uthenga wachilimbikitso koma sichinakwanire. Madala akadandiyankhula mwina ndikadalimba mtima kuti akupeza bwino. Usiku ndinapita kunyumba kukagona mtima uli wosweka ndithu. Unali usiku wautali. M'mawa kutacha pa 19 ndinapita kukawazonda. Sindinaopne kusintha kwenikweni. Mantha anandigwira ndipo ndinadziwa kuti madala sadzandiyankhulanso. Usiku wa pa 19 unandisautsa kwambiri. Sindinagone. M'mawa pa 20 July. Kutacha m'mawa ndinamva mauthenga akuti dziko la Malawi lili pamoto. Anthu anali kuchita zipolowe zosonyeza kukwiya ndi ulamuliro wa dziko lino. Mkazi wanga anali ali ku Mzuzu ndipo anandiuza kuti wakwera basi m'mawa koma akulephera kutuluka mumzindawu chifukwa cha mfuti zimene zinali kulira. Nkhawa inandigwira. Ndinamvanso kuti ku Lilongwe, ku Blantyre ndi maboma ena zinthu sizinali bwino. M'tawuni ya Mchinji munali bata ngakhale kuti m'misewu munali apolisi ochuluka kuposa nthawi zonse. 12 Koloko Masana Nthawi yowonera odwala itakwana cham'ma 12 ndinanyamuka kuti ndikazonde madala. nditatsala pang'opno ndinamva foni ya amayi kundiuza kuti ndifulumire. Mtima wanga unagunda, thupi linachite tsembwe! chongofika m'chipinda momwe munagona madala nkhope ya amayi inandiuza zonse. "Aliki bambo ako ulendo uwu"! Inali nthawi yowawitsa m'moyo mwanga! Ndinayandikira ndikuwagwedweza madala koma sanasunthe ngakhale pang'ono! Apita madala! Tsopano chaka chaka chatha. Madala anagona ku Mchinji mwakufuna kwawo. Sanafune kubwerera kwawo ku Chitundu ku Dedza. Ku Mchinji anasamukirako 1995 atapuma pantchito. Ku Mchinji kuanasanduka kumudzi kwawo, kumudzi kwathu. Anali ndi abale andi abwenzi ambiri. Onse anachitira umboni patsiku lowasunga madala pamene anafika mu unyinji wawo. Kufika kwa unyinji umenewu kunandikumbutsa ndipo kudzapitiriza kundikumbutsa moyo wa madala - kuseka ndi aliyense! Madala anali munthu wokondwa nthawi zonse ndipo ndiyamika Mulungu chifukwa cha mphatso imeneyi. Akanakhala wopanda mphatso imeneyi mwina bwenzi pano tikukamba nkhani ina. Ndi chikhumbokhumbo changa kuti ndikumbukire moyo wa bambo anga pofotokoza zina zimene zinawathandiza kukhala moyo wosangalala ngakhale atakumana ndi mavuto amtundu wanji pamoyo wawo. Tinakhalapo moyo wovutika kuthupi koma mu mtima mokha tinali anthu osangalala, achimwemwe nthawi zonse chifukwa cha madala. Mzimu wanu uziusa mumtendere Madala ndipo ngati kumene muliko ngati n'kotheka kuchita nthabwala nkumaseka, pitirizani mpaka tidzaonanenso nkusekera limodzi!