Friday, April 4, 2014

Kwathu

Muno m'tawuni timangowonana. Anthufe tonse tli n'kwathu. Ena kwawo n'kumagomo, ena kwawo n'kunyanja, ena kwawo n'kuthegere, ena kwawo n'kuntherero kwa jiko, ena kwawo n'kumusha, ena kwawo n'kuthoni. Nthawi zina kwawo kwa munthu kumapanga munthu kuti akhale momwe alili. N'chifukwa chake nthawi zina ukadabwa ndi momwe akuchitira zinthu kapena momwe munthu wina akuyankhulira timafunsa ndithu kuti kwanu n'ku? Nanga inu kwanu n'ku. Ine kwathu n'kumsewu, ko Mbuna. Nkhani ya kwanu pena pake imakhala yovuta pa zifukwa zosiyanasiyana. Anthu amasintha kwawo pa zifukwa zosiyanasiyana: kusamuka, maphunziro, ntchito, ndale, malonda, banja ndi zina zambiri. Ife zonsezo tadutsamo koma kwathu sikunasinthe. Kwathu n'ko Mbuna. ndipotu kwanu ndi kwanu, ngakhale kutaoneka kosasangalatsa m'maso mwa anthu ena, kwanu ndi kwanu basi. Ine kwathu n'ko Mbuna, ku Mpenu ko Mazengera ku Nkhoma. Mudzi wathu uli m'mphepete mwa msewu waukulu wochokera ku Lilongwe kupita ku Blantyre pa mtunda wa makilomita 40 kapena mamayilosi 25 kuchokera mumzinda wa Lilongwe. Mudzi wathu wayandikana ndi midzi ina monga Bokonera, Mng'ona ndi Mdzinga. Kukhala pafupi ndi msewu waukuluwu ndi chinthu chimodzi china chimene timachinyadira kwambiri pa zifukwa zambiri. Mwachitsanzo, mayendedwe sizovuta. Kungokhala m'mbali mwamsewu nthawi ina iliyonse upeza galimoto yokwera kupita komwe ukufuna. Kulibe kabaza kwathu! Chokhacho ndimachinyadira kwambiri. Tikafuna kukamba za malonda a mumsewu ndiye pali nkhani koma siyabwalo lino! Mwina ena n'kumangomangonena za kwawo chikhalilenicho kwawoko sanakhaleko. Ife kwathu tinakhalako ndipo tikukudziwa bwino. Ine kwathu ndinakhalako ndithu ndipo ndimapitako zedi. Pa ubwana wanga ndinakhalako pamene ndinaphunzira sukulu, sitanadede 1 kenako pamene ndinali sitandede 5. Sitandede 1 ndinaphunzira pa sukulu ya Kaundama yomwe masiku a m'mbuyomo makamaka cha m'ma 1980 inali yotchuka kwambiri ndikusankhitsa ana opita ku ku sekondale. ndi zinthu zochepa zimene ndimazikumbukira pamene ndinali mu Sitandede 1 chifukwa mwina ndinali wachichepere. Koma pamene ndinabwereranso kumudzi kukaphunzira Sitandede 5 pali zinthu zambiri zimene zinakhazikika m'mutumu. Zina ndi monga anzanga amene ndinkasewera nawo kunyumba komanso kusukulu, zakudya ntchito komanso zosangulutsa zina monga zilombo! hahahahahaha! Pali anzanga ambiri amene ndinadziwana nawo nthawi imeneyo amene ngakhale pano timacheza kwambiri. Mnzanga woyamba ndi malemu Tenderetu (Sosten)... mzimu wake uziusa mumtendere. Za iyeyu ndinalemba kale. Tenderetu anali msuwani wanga amene anandilandira nditangofika kumudzi. Kuchokera tsiku limenelo tinkayenda ngati inswa. Ndidzamukumbukira mpaka kale Tenderetu! Amayi anga ndi Omama (mukafika kwathu adzakuwuzani kuti Omama ndani. Olipo omodzi basi). M'bele mwawo anabadwa ana asanu, amuna atatu, akazi awiri (Omama ndi Omayi). Panopa amayi anga amakhala ku Mchinji pa Boma m'mudzi mwa Robert. Koma ngakhale makolo anasamukira ku Mchinji mçhaka cha 1995, kwathu ndi ko Mbuna ndithu. Ngakhale mudzi wathu sukuoneka kusintha kapena kutukuka, ndimanyadirabe kuti ndiko kwathu ndipo ndimakhulupirira kuti sindikadakhala momwe ndilili chipanda kubadwira ko Mbuna.Tikafika kwathu amati kwabwera Oyaliki kapena o ku Zomba. Kwathu ko Mbuna. Inu kwanu nku?

No comments: