Wednesday, December 10, 2008

Malawi Dziko Lokongola






AMalawi anzanga, munthune ndimanyadira kuti ndinabadwira ku Malawi kuno. Poyamba ndinkasiririra ntakhala wakunja. Maganizo amenewa amabwera kamba kowonera kanema wowonetsa malo osiyanasiyana akunja kwa dziko lino. Makanemawa amangowonetsa zoipa zokhazokha za dziko lino ndi mayiko ena a kuno ku Africa. Koma nditayendera maboma onse a dziko lino ndinaona kuti Malawi ndi odala kwambiri kuposanso mayiko ena amene timawasirira. Kuli mapiri kunja kuno. mitsinje, nkhalango, nyama, nyumba, anthu okongola, magule (virombo), zigwa, ndi zina zambiri. Patsamba lino ndikhala ndikulembapo za malo ena amene ndidafikako m'dziko muno. Mwa malo amene amandichititsa chidwi kwambiri ndipo ndimawakonda kwambiri ndi boma la Chitipa, nyanja ya Malawi ndi phiri la Mulanje.

2 comments:

Unknown said...

What happened to this. Wow I love the idea

Unknown said...

This was and is a beautiful project