Wednesday, July 14, 2010

Mnzanga, Happy Wapita

Dzulo madzulo nditaweluka kuntchito monga mwachizolowezi ndinapita kokachita masewero olimbitsa thupi. Ndinabwerako cha m'ma7koloko usiku. Nditafika kunyumba ndinanyamula chisusu changa kuti ndikadzithire madzi kuchotsa chitungu. Polowa kuchipinda chogona ndinasangalala koposa chifukwa ndinapeza a Nyagondwe akundisitila zovala. Nditangolowa kubafa ndinamva kuyitana kuchokera kwa mayi. Ndinatuluka kuti ndikamve kuyitanako.

"Kodi paja Happy dzina la abambo ake ndani? anandifunsa nditangosuzumira pakhomo la kuchipindako. "Nyirenda?" Anapitiriza kufunsa ndisanayankhe funso loyamba lija.

"Ee, bwanji?" ndinafunsa ndi chidwi.
"Wamwalira, akulengeza pa wayilesi kuti Happy Chokoma Nyirenda wa ku Nkhatabay amene amadwala kuchipatala cha Zomba wamwalira."

"Hiii Happy inu. Mpaka wamwalira ndi mutu womwe uja" Ndinasendera ndikukakhala pa bedi kuti mtima ukhazikike.

Happy anali mnzanga ndipo tinadziwana m'chaka cha 2003 kuno ku Zomba. Tinadziwana chifukwa cha mnzanga wina Jonah Mphanda amene ine ndinaphunzira maye ku sekondale ku Mtendere. Panthawiyo Jonah ndi Happy ankagwira ntchito ku Interaide. Kenaka awiriwa anasiya ntchito ku Interaide ndipo Happy anayamba kugwira ntchito ku Spar.

Sabata zitatu zapitazo, Jonah anandiyimbira foni kundifotokozera kuti Happy wagonekedwa kuchipatala ndipo akudandaula mutu. Tsiku lomwelo ndinapita kukamuona ndipo tinacheza nandifotokozera kuti mutu ndi umene ukumusautsa koposa. Ndakhala ndikukamuona koma zimaoneka kuti matendawa sanasinthe mpaka pamene dzulo chakum'mawa amamwalira.

Happy amachokera ku Nkhatabay. Ndidzamukumbukira Happy chifukwa chokonda kuseka ndi nthabwala. Tikakumana timakonda kukamba zoselewula ndipo mwa dzina lake iye anali wosangalala nthawi zonse.

Mzimu wako uwuse mu Mtendere Happy.

No comments: