Monday, July 19, 2010

Mwana wanzeru akondweretsa makolo




Kutsiriza maphunziro ndicho chinthu chimodzi chopambana m'moyo wa munthu. Iyi ndi nthawi imene munthu amatsiriza osangoti maphunziro okhawo ayi, komanso gawo la moyo limene wakhalamo nthawi yaitali ndithu. Komanso ndi nthawi imene munthu amayembekezera kuyamba moyo watsopano. Iyi imakhalanso nthawi yodziwunika ndikudzisanthula pamene unachita bwino komanso pamene sunachite bwino kuti mwina m'moyo wina umene ukukawuyambawo ukachite mosiyana ndi m'mbuyomo. Komanso imakhala nthawi yolingalira za moyo watsopano uli nkudza. Pachifukwachi ena amakhala ndichimwemwe poganizira kuti mwina tsopano asiyana ndi moyo wovuta ndipo akukayamba moyo watsopano. Koma ena amakhalanso ndi nkhawa kuti mwina akukayamba moyo wovuta kusiyana ndi wam'mbuyomu.

Ndikumbuka kuti pamene ine ndinali kutsiriza moyo wa ku sekondale, ndinali ndi chimwemwe kuti tsopano sindidzasambanso madzi ozizira m'mawa ndipo ndizidzadzuka nthawi imene ndikufuna. Panthawiyi ndinaona kuti tsopano ndapeza ufulu wochuluka ndipo moyo wa ku sukulu ndinawuona ngati ukapolo. Komabe ngakhale izi zinali chomwechi, ndinalibe ndi nkhawa pa za moyo wam'tsogolo. Choyamba chinali chakuti kodi mayeso ndikhoza? Nanga ndikhoza bwanji? Ngati sindikhoza bwino, ndidzachita chiyani? Kodi ndidzapeza mwayi wa ntchito? Idzakhala ntchito yanji? Ndizidzalandira ndalama zingati? Nanga ngati ndikhoza bwino, ndidzasankhidwa kupita ku Yunivesite? Kodi ndikasankhidwa kupita ku Yunivesite ndikachita maphunziro anji, nanga adzandipatse malipiro a sukulu ndani? Kodi ndikakhoza n'kudzapeza ntchito yapamwamba? Ndikhukupirirra awa ndi ena mwa mafunso amene achinyamata amene akukonzekera kutsiriza maphunziro awo nthawi ino akulimbana ndi kupeza mayankho ake.

Dzana Loweluka pa 17 July linali tsiku lotsanzikana ndi ophunzira a Fomu 4 pasukulu ya Mlanda ku Ntcheu. Tinayitanidwa ndi mwana wathu Priscilla kuti tikhale nawo pamwambowu. Sitinachione chofunikira kuti tichoke ku Zomba kukafika ku Ntcheu chifukwa cha mwambo umenewu chifukwa panthawi yathu makolo sankaitanidwa ku mwambo wamtunduwu. Komansotu panthawiyi ophunzirawa amakhala asanalembe mayeso awo ndipo sakudziwa ngati adzakhoze kapena ayi. Koma mwanayu anachonderera ndithu kuti ife tipite ndithu tikaonelere mwambowu.

Ndinanyamuka ku Zomba cham'ma 8 koloko m'mawa pamodzi ndi Onyamata ndipo tinafika ku Mlanda cham'mapasiti 10. Titangofika Priscilla anatithamangira akusekerea kudzatilonjera. Apatu n'kuti akukonzekera kulowa mu Holo imene mumachitikira mwambowu. Kenaka mtsikana wina anabwera kudzatitenga n'kutilowetsa muholomo. Kunabweratu makolo ambiri komanso anthu oyimira magulu osiyanasiyana monga mafumu (a T/A Masasa anali kumeneko), a mpingo komanso abizinesi. Mwambo wake unali wosangalatsa kwambiri. Kunali magule, kuyimba, masewero ndi zochitikachita zambiri. Alendo onse pamodzi ndi ophunzira analandira chakudya ndipo chinthu chosangalatsa makolo kudyera limodzi ndi ana awo kusukulu.


Ine ndinasangalala koposa kuona kuti mwana wathu anali mmodzi wochita nawo masewero. Mwana wathu ndi wofatsa kwambiri moti sitinkayembekezera kuti angathe kuyima pagulu la anthu n'kukamba zomveka. Koma ayi ndithu patsikuli iye anali kuchita gawo lowulutsa mawu kunyumba ya mphepo ya Zodiak! Ndinakondwera kwambiri. Koma nthawi yopambana kwambiri imene ine ngati kholo sindidzayiwala chifukwa ndinazizwa kwambiri inali pamene anali kupereka masatiketi kwa ana amene anachita zinthu zopambana panthawi imene anali pasukulupa. Masitifiketi oyamba anaperekedwa kwa mwana aliyense amene anali kutsiriza maphunziro ake pa sukulupa. Koma gulu lachiwiri la masatifiketiwa linali operekedwa kwa okhawo amene anachita bwino kuposa anzawo mu gawo lina lake monga pa phunziro lililonse, mavalidwe, mayimbidwe, ndi zina. Zinali zoseketsa ndizosangalatsa kumva kuti wina anasankhidwa kukhala wolawirira pochita china chilichonse, komanso wina anasankhidwa kukhala munthu wokonda kulangiza anzake. Panalinso mwana wina amene anasankhidwa kuti amakonda kumwetulira ndi kusekerera nthawi zonse. Mwana ameneyu ndi wachimwemwe ndipo kwake nkuseka basi. Mayi ake ndimawadziwa ngatinso munthu wokonda kuseka ndikuseketsa moti sindidadabwe nditamva kuti anasankhidwa kukhala munthu womwetulira nthawi zonse. Panalinso kamtsikana kamene kanasankhidwa munthu wodziwa kuyimba. Mwana ali ndi nthetemya uyo. Atalandira satifiketi yake anapemphedwa kuti angotilawitsako pang'ono luso lake. Holo yonse inamumbera m'manja mwanayu atangoyimba ndime imodzi yokha.

Tsopano olengeza mayina anali kufika kumapeto wa mndandanda ndipo ine ndinali kuganiza zonyamuka poganiza kuti mwambo wopereka masatifiketi tsopano watha. Kenaka ndinangomva kuti “wophunzira amene anachita bwino kuposa onse mu phunziro la Chingerezi, Priscilla Chimtolo.” Ine mtimawu unangoti myuuuu! Ndinadzidzimuka koposa ndipo sindinakhulupirire. Nditacheukira pamene anakhala Priscilla ndinangoona kamwana kanga kakubwera kali mwee kudzandikupatira. Ndinali ndi chimwemwe chodzadza tsaya. Ndinali ngati ndikulota. Ndinaonanso kuti naye ali wosangalala kwambiri kuti anapata mphoto imeneyi komanso chifukwa chakuti ine ndinafika kudzachitira umboni mwambo umenewu. Pamene ndimanyamuka ndinali munthu wosangalala ndipo njira yonse ndinayenda ndi chimwemwe chokhachokha. Ndili ndi chikhulupiriro kuti zimenezi zimuthadiza Priscilla komanso ana ena onse amene anachita bwino kuti alimbikire kuti pamayeso awo otsiriza adzachitenso chimodzimodzi. Mwana wanzeru akondweretsa makolo.

No comments: