Friday, July 9, 2010

oTenderetu


Nthawi zina ndikakhala phe, nzeru zimandithera ndikaganiza kuti kodi imfa imabwera bwanji pamoyo wamunthu ndipo kuti kodi analenga imfa ndani? Nanga kodi munthu akafa amapita kuti? Mwina nthawi zambiri pamene tili ndi moyo wangwiro, zonse zili myaaa timayiwalako zoti kunja kuno anthu amafa n'kutsikira kuli chete osadzamutemanso gaga. Koma zovutazi zikagwa pakati pathu mpamene timadzidzimuka n'kumati kodi paja moyowu umatha ndithu. Ine ndimaona kuti nthawi imene mnzathu akuyikidwa m'manda ndiyo nthawi yowawitsa chifukwa umakhala umboni woti basi mnzathuyu apa lake watseka. Nthawi zambiri ikafika nthawi imeneyi misozi imatsika ndithu ngakhale malirowo akhale kuti sakundikhudza kwenikweni. Imfa imene mpaka pano imandipweteka kwambiri ndi yamzanga, msuwani wanga, mchimwene wanga, Tenderetu (Tiyenderetu). Imfa imeneyi imandipatsa maganizo ndi mafunso ambiri amene mpaka lero sinditha kupeza mayankho ake.

Ine ndi Tenderetu tinadziwana m'chaka cha 1983 kumudzi kwathu ko Mbuna ku Lilongwe. Chaka chimenecho makolo anga anaganiza zoti mayi anga pamodzi ndi ine komanso mng'ono wanga Gregory ndi alongo anga Jestina ndi Chisomo tipite kumudzi kuti amayi akayang'anire ntchito za kumunda ndipo ife tikaphunzire sukulu komweko. Iyi ndi nthawi ina yowawitsa m'moyo mwanga chifukwa mpaka pano sindimvetsa chimene makolo anga anachitira zimenezi, kutisiyitsa sukulu yapamwamba, nyumba ndi moyo wabwino kupita kumudzi. Iyitu inalinso nthawi imene kunabadwa abale anga ena awiri amapasa, Symon ndi Sibongire. Kubadwa kwa ana amenewa sindidzakuyiwala chifukwa ine ndi amene ndinali mlezi wothandiza amayi anga. Lachitatu lililonse ndinkajomba kusukulu kuwaperekeza amama kusikelo ya anawa ku Chipatala cha Nkhoma chomwe chili pamtunda wa makilomita pafupifupi 10 kuchokera kwathu.

Titangofika kumudzi ko Mbuna kuchokera ku Dzalanyama Forest komwe bambo anga ankagwira ntchito panthawiyo, tinaona zinthu zambiri zosintha chifukwa aka kanali koyamba kwa ife kukhala kumudzi motero sitinasangalale nkomwe kuti tizigona m'nyumba ya udzu, kukakhala pansi kusukulu pamene tinasiya abambo okha m'nyumba yabwino ya malata. M'mawa kutacha ndinapita kukakhala pakhonde la nyumba ya agogoa anga okondedwa, Onganga (mzimu wawo uziwusa mumtendere ndipo ndidzalembanso za gogo ameneyu, amene ndimamukumbukira nthawi zonse chifukwa cha mtimwa wake wachifundo. Timakusowani Onganga). Ndikuothera kadzuwa pakhonde paja ndinaona kamnyamata kamsinkhu wanga katakhala pakhonde la nyumba ya Omayi (achemwali a amayi anga). Maso athu atangoti tha, tonse tinamwetulirana chifukwa tinazindikirana.

Tenderetu anali mphwawo wa bambo anga aakulu. a Mapondera (amuna a Omayi, achemwali a amama). A Mapondera ankachokera ko Mdzinga mudzi umene uli tsidya lina la mudzi wathu kungodumpha msewu wawukulu. Iwowa anali kukhala m'mudzi mo Mbuna ngati kuchikamwini. Amayi a Tenderetu anamwalira pakati pa 1980 ndi 1981. Choncho atangomwalira mayi ake, amalume akewo, aMapondera, anamutenga iye pamodzi ndi abale ake Nana ndi Maseko kuti azikakhala nawo ku Chongoni Forest ku Dedza komwe iwo ankagwira ntchito panthawiyo. Abambo anga anagwirakonso ntchito ku Chongoni ndipo ndikumene ine ndinabadwira koma tinasamukako 1980 kupita ku Dzalanyama. A Mapondera atapuma ntchito 1982 anakakhala kumudzi ko Mbuna pamodzi ndi mwana wawo Richard ndi aphwawo aja, Tenderetu, Nana ndi Maseko.

“Alick” anandiyitana Tenderetu nandikodola. Nthawi yomweyo ndinapita kukamupatsa moni ndikumufunsa kuti ali kalasi yanji. Iye anali sitandede 3 pamene ine ndinali sitandede 5. M'zaka zakubadwa iye anali wamkulu ndi zaka ziwiri koma tinali ofanana misinkhu. Kuchokera tsiku limenelo Tenderetu anali mnzanga waponda apa ine mpondepo. Sitinkasiyana kulikonse. Kusukulu tinkapitira limodzi, kuwelukira limodzi, kusewerera limodzi, kudyera komanso kugonera limodzi. Nthawi imeneyo tinkagona kumphala pamodzi ndi amalume anga aChadza. Usiku pogona tinkafunda bulangete limodzi, ndipo nthawi zambiri timacheza mpaka mwina aChadza kumachita kutiletsa kuti tigone. Panthawiyi n'kuti iwowo anali mu sitandede 8 koma anali kubwereza kachisanu ndi katatu. Tikakondwa kwambiri tinkafika pomaphaphalitsana makofi kapena kutibulana zibakera ndithu mpaka wina athawe. Izi zinkangokhala zosewera ndipo sitimadana ngakhale wina atamenya mnzake kwambiri. Nthawi yamango itakwana ine ndi Tenderetu tinasula timipeni kuchokera ku misomali ya 12 ichesi kuti tizikasendera maboloma. Timati tikangokonza kuti lero tikakhaulitsa mango timayambira ku Bathe (kumunda kwathu), kuchoka apo tili ku kuseli kwa Bathe (kumunda kwa Omayi) mpaka kukamalizira ku Dondo (kumunda kwa amalume ake a Tenderetu). Tikamabwera kumeneko mimbazi zili mzuu, kukhuta, pakamwapa pali noninoni, m'manja monsemu midondolozi ya madzi a mango italemberera. Tikatero ndiye kuti nsima yamadzulo kumangokhala kuyikandakanda basi usiku kumangogeya ndi kutuluka panja kukataya madzi.

Kumapeto a chaka chimenecho titatsekera sukulu komanso titakolola dzinthu abambo anga ananena kuti tonse tibwerere ku Dzalanyama. Inali nthawi yovuta kwa ine kuti ndisiyane ndi mnzanga wapamtima. Komabe sindafune kuphunziranso kumudzi. Nditafika ku Dzalanyama ndinamulembera Tenderetu kalata kumufotokozera momwe ndinayendera. Koma nthawi imeneyo kunali kovuta kuti tizilemberana makalata pafupafupi chifukwa tinali pamsinkhu umene sitinkatha kudzipezera ndalama zogulira masitampa. Kwa zaka zitatu ine sindipitenso kumudzi ndipo sindinaonanenso ndi Tenderetu.

M'chaka cha 1986 abambo anga ananditenga kuti akandionetse kwawo ku Chitundu ku Dedza. M'banja mwathu palibe amene ankadziwa kwawo kwa abambo anga ndipo amayi akuti anapitako kotsiriza m'chaka cha 1976. Choncho ine ndinasangalala kuti ndidzapita kukaona kwawo kwa abambo anga chifukwa kunali abale awo amene ankakonda kudzationa koma ife tinali tisanaone kumene ankachokera. Popita kumeneko tinayima kumudzi ko Mbuna. Aka kanali koyamba kuonana ndi Tenderetu m'zaka zitatu. Pochoka ku Chitundu ine ndinatsalira kumudzi kuti ndichezeko ndi mnzanga. Tonse tinali titakula tsopano, zosewera zathu zinali zitasintha. Panalibenso zomenyana. Tsopano timangosewera mpira basi. Panthawiyi n'kuti Tenderetu atasintha dzina, kukhala Sosten. Komanso anali atameta kugule ndye ena ankamuyitana kuti oTenderetu kapena oSositeni monga mwa mwambo wake. Amalume ake anamwalira chaka chomwecho (1986) m'mwezi wa March. Koma pamene ankamwalira n'kuti atamupatsa ndalama yoyambira bizinesi yogula mafuta a galimoto kwa magalimoto odutsa mumsewu popeza mudzi wathu uli m'mbali mwamsweu wawukulu wa Blantyre-Lilongwe. Iyi inali bizinesi imene inali yolula oanthawi imeneyo. Panthawiyi nkuti amalume ake atasamuka m'mudzi ndikukamanga nyumba yaikulu m'mbali mwa msewu. Amalume ake asanamwalire anapempha oMayi kuti iwo akadzamwalira adzasunge ana onse atatu amasiye) Tenderetu, Nana ndi Maseko). Choncho Tenderetu anapitiriza kukhala ndi oMayi komanso msuwani wake weniweni, Richard. Ndinapemha kuti chaka chimenecho ndiphunzire kumudzi komweko koma abambo anga anandikaniza. Nditacheza kwa mwezi umodzi ine ndinabwerera ku Dzalanyama kukapitiriza sukulu. Nditalemba mayeso a Sitandede 8 mu 1987 ndinapempha kuti ndikachitenso tchuthi kumudzi ndipo anandiloleza. Chaka chimenecho tinacheza kwambiri ndi Tenderetu. Apatu tsopano iye anali kupeza ndalama zambiri chifukwa cha bizinesi ija. Nthawi zina ndinali kumuthandiza kukochola magalimoyo komanso kupopa ndikunyamula mafuta. Chaka chotsatira ine ndinasankhidwa kupita ku Mtendere secondary school ku Dedza. Uwu unali mwayi wanga chifukwa ulendo uliwonse popita ndipobwerera kusukulu ndimayima kumudzi kwathu kwa masiku angapo ndipo izi zinandipatsa mwayi womacheza ndi Tenderetu pafupipafupi mpaka nditamaliza maphunziro anga mu 1992. Nthawi zina popita kusukulu ankandipatsako ndalama zokadyera ndipo ulendo wina anandigulirako malaya. Ndinanyadira koposa.

Nditangolemba mayeso anga a Fomu 4 ndinapempha makolo anga kuti ndikadikire mayeso kumudzi. Iwo anandilora ndipo ndinasangalala kwambiri. Nthawi imeneyi ndinamuthandiza kwambiri Tenderetu pa bizinesi yake ya mafuta. Analinso kugula ndi kugulitsa mbewu, ufa ndi zinthu zabiri zopezeka m'magalimoto odutsa. Tenderetu sanasowe chilichonse. Anali kusamalira pakhomopo tsopano ndiye. Anali wopatsa kwambiri. Mudzi wonse unamudalira. Iye anali wakhama pantchito ndipo samalola zibwana kapena zaulesi. Panthawiyi n'kuti Sadam Husein yemwe anali mtsogoleri wa dziko lija la Iraq atatchuka kwambiri chifukwa chokaputa dziko la Kuwait m'chaka cha 1990. Tenderetu anali munthu wokonda kumvera wayilesi kuti azimva zomwe zikuchitika kunjaku. Kulimba mtima kwa Saddam kunamusangalatsa ndipo chifukwa chakuti naye sanafune kuti anthu azimutola poti ndimwana wolemera anadzitcha kuti Sadam. Iye sikuti anali waukali kapena wokakala moyo ngati Sadam koma anamusilira Sadam chifukwa cholimba mtima. Dzina la Sadam anatchuka nalo kwambiri.

Mayeso anga atatuluka ndinasankhidwa kukapitiriza maphunziro ku Chancelllor College. Apa tsopano ndinadziwa kuti tidzatalikirana ndi Tenderetu. Chaka chomwecho iye anasiya sukulu mu Sitandede 8 ndikupitiriza bizinesi yake. Anapeza malo ake ndikumangapo nyumba. Mu 1995 Tenderetu anakwatira. Ukwati unachitika ndili kusukulu motero sindinathe kukhala nawo. Ndinakhumbira kwambiri. Ngakhale Tenderetu anakwatira, anapitiriza kuthandiza oMayi komanso anthu ambiri am'mudzi mwathu ngakhalenso achilendo. Anapala maubwezi ambiri chifukwa cha bizinezi yake. Analimbikira kulima komanso kugula mbewu zosiyanasiyana. Atazindikira kuti bizinesi ya mafuta inali yosadalilika chifikwa cholondedwa ndi apolisi iye anaganzia zotsekula sitolo. Anamanga sitolo yake yayikulu momwe munali katundu wosiyanasiyana. Anthu ambiri anali kudzagula katundu ena pangongole. Tsiku lina tikucheza nditapita kukamuona kuchokera ku Zomba anandiuza kuti nthawi zina saona kufunika kwa maphunziro chifukwa aphunzitsi amene an'kamuphunzitsa ku pulayimale anali kuvutika kwambiri ndipo kuti ena mwa iwo anali kulephera kubweza ngongole zimene anakatenga musitolo yake. Iye ananena kuti ana sangalimbikire sukulu ngati aphunzitsi akukakongola ndalama kwa anthu amene sanapitirize maphunziro. Pena ndinagwirizana naye makamaka ngati timapita kusukulu kuti tidzakhalae ndi moyo wabwino. Koma nkhani ya aphunzitsi ndi ina yapadera. Tenderetu anali ndi mfundo zake ndipo anali wokonda mtsutso pa nkhani zosiyanasiyana. Chinthu china chimene iye ankakanitsitsa kuti sangachite ndiye kusunga ndalama zake ku banki. Mawu ake anali akuti iye saona chifukwa choti azikakhalira pmazele chifukwa cha ndalama zake zomwe.

Pasitolo pake panali pachibulo. Sipankasowa munthu. Panali posewerera ntchuwa, panali pogulitsira nzimbe, nthochi, panali pomwera fanta, panali powusira anthu apulendo. Ena mwa iwo maka oyenda panjinga kuchokera mitunda ya Chitundu anali kusungitsa njinga zawo n'kukwera magalimoto wa m'tawuni. Tenderetu anali mlerakhungwa chifukwa sanasankhe anthu ocheza nawo, akulu, ana, achinyamata, olemera, osauka, owadziwa, achilendo. Chifukwa cha mtimawu anthu tsopano anamutcha Bakili. Chifukwa cha ichi, anthu anamudalira koposa. Anamusankha kukhala wapampando wa sukulu komiti komanso wapampando wa chipani ku Bathe Area. Uwutu sunali udindo wamba. Nthawi imeneyo phungu woymira derali anali Wolemekezeka a Louis Chimango moti pamene iwowa anali kuyendera derali aakuluakulu ake amene amayenda nawo anali a Tenderetu. Chinali chinthu chopambana kuwona mnzanga atafika pamenepa. Nthawi zambiri tikamacheza anali kukamba nkhani za ndale ndi chidwi ndipo kawirikawiri anali kufuna kudziwa kuti ine ndili mbali iti chifukwa chakuti ndimakhala kummwera. “Ndale zikuyenda bwanji kum'mweraku?” Ankakonda kufunsa choncho tikakumana. Iye ankakonda kupitiriza kunena kuti, “kunotu ndiye ndi Kongiresi basi, ife onzathu ndoChimango basi, tambala wakuda! Ochawa songawine kuno” Tikatere tinkaseka.

M'mwezi wa July, 2004 mwana wanga atagonekedwa kuchipatala . Tsiku lina chakumadzulo ndinkakonzekera kukamuona mwanayu pamene ndinalandira telefoni yochokera kwa mchimwene wanga Richard Mapondera amene ankakhala ku Blantyre. 'Tenderetu wamwaliratu" anatero Richard, mosisima. 'Wagundidwa ndi galimoto..." anapitiriza. Ndinaponya foni pansi n'kulowa kuchipinda. Ndinalira mokweza. Thupi langa lonse linanyowa ndi chitungu cha chisoni ndi mantha. Sindinakhulupirire kuti zingatheke kuti mnzanga Tenderetu n'kumwalira. Patatha ola limodzi ndinatuluka kuchipinda n'kunyamuka kupita kuchipatala kukaona mwana wanga. Nditafika, mkazi wanga anandilandira ndichimwemwe kufuna kunditsimikizira kuti mwana anali kupeza bwino tsopano. Koma anadabwa kuona kuti misozi inali kutsika m'masaya mwanga. Anandigwira n'kundiuza kuti ndisade nkhawa mwana ali bwino ndipo amatulutsa tsiku lotsatira. Ndinamuwuza kuti Tenderetu wamwalira. Sindinathe kuwagwira mawu ndipo izi zinadabwitsa anthu ena onse m'chipatalamo chifukwa anayamba kuganiza kuti mwina mwana uja wamwalira. Tinatuluka panja.

M'mawa, Richard uja anabwera kudzanditenga pa galimoto yake kupita kumudzi. Njira yonse tinayenda mwachinunu. Titangowoloka Diamphwe tonse misozi inayamba kutsika. Galimoto isanayime nkomwe azimayi anali atayiwunjirira uku akuloza tsidya lamsewu akulira mokweza. Zinali zomvetsa chisoni. galimoto yonyamula mowa wa Chibuku imene inatenga moyo wa mbale wanga inali gada! tsidya la msewu moyang'anana ndi siwa. Mtima wanga unasweka ndipo ndinalakala nditakangoyatsa galimotoyo. Azimayi analira mokweza ngati akuti 'chonde kabwezereni ku chigalimotocho.' Titapuma tinakazungulira galimotoyo yomwe tsopano apolisi anali kuyilondola powopa mkwiyo wa anthu.

Imfa ya Tenderetu inali yomvetsa chisoni. Patsikulo, akuti chakum'mawa kunafika galimoto yogulitsa buledi kuchokera ku tawuni ku Lilongwe. Ndipo ogulitsa bulediwo sanamupeze Tenderetu ndipo anangosiya buledi n'kunena kuti ndalama adzatenga madzulo popotoloka kuchokera ku Dedza. Galimotoyo inabweradi madzulo cha m'mapasiti 6. Inamupeza Tenderetu ali m'nyumba ndipo atamva hutala iye anatuluka ndi mwana wake m'manja kukayankhulana ndi wogulitsa buledi uja. Atauzidwa mtengo wa buledi amene anasiyayo iye anabwerera m'nyumba kukatenga ndalama. Pobwerera mwana uja anamusiya ndi amayi ake. Atafika pagalimotopo anaona kuti mbali inayo yamtunda wa Lilongwe kunali kubwera galimoto yonyamula mowa wa Chibuku yomwe inali pa liwiro lalikulu komanso linali litataya mbali yake nkulunjika mbali imene inayima galimoto ya bulediyo. Ataona izi, Tenderetu anaganiza zothawira mbali inayo. Asanamalize n'kudmphira mbali inayo, chigalimoto chija chinamuvungira limodzi, kum'khwekhwereza n'kukamuponya pafupifupi pamtunda wa malipande 100 uku chigalimotocho chikunkhulira mpaka kukagudubuzika m'munda. Mdima n'kuti utagwa. Ndiye kunali kuyitana kwinaku anthu akusaka Tenderetu. Pamene Tenderetu amapezeka kumizele anali atamwalira ndipo thupi lake litanyenyeka kwambiri. Adapita n'chigalimoto Tenderetu.

Kunali namtindi wa anthu patsiku loyika maliro a Tenderetu. Anthu anapereka maumboni a moyo wa Tenderetu. A kumpingo, kusukulu, abizinesi, kuchipani komanso makasitomala. Ena odutsa pamagalimoto awo amati akamva zoti malirowo anali a Tenderetu anali kuyima kukhuza nawo ndikusiya chipepeso. Ambiri anabwera kudzakhala nawo pamwambo woyika malirowo. Mwa anthu ongodutsawo wina anapempha kuti ayankhuleko m'malo mwa anthu ena onse amene ankamudziwa Tenderetu. Iwo anali kungodutsa paulendo wawo wopita ku Lilongwe koma anayima ataona kuti pachitika zovuta. Atamva kuti womwalirayo anali Tenderetu, sanamvetse. M'kuyankhula kwawo iwo anati: “ife tatayika chifukwa cha imfa imeneyi. Ife mwana uyu ankang'unga mnzathu, sankaona kuti tachokera kuti, tavala chiyani, tili ndi chiyani, koma an'kangotilandira n'kumacheza nafe ngati akucheza ndi anzake. Timayima panyumba pakepa n'kumwa madzi, kusungitsa njinga zathu n'kumapita ulendo wa ku Lilongwe, pobwera amatilandira mwaulemu. Ndiye lero n'kumati Tenderetu wamwalira? Tatayika ife! Bakili wathu wapita, ineee! Tikapumira kuti ifeee..." ndiye panabukatu chiliro; “Bakili wathu wapita, Bakili wathu watisiya ife.”

Lero pamalo a Tenderetu ndi pabwinja pomvetsa chisoni. Mkazi wake anabwerera kwawo ndi ana ake atatu ndipo anakwatiwanso ndi mwamwuna wina. Mng'ono wake, Maseko anatsala pamlopo anagulitsa malata zitseko ndi katundu wina yense amene anasiyidwa. Naye anamwalira atamenyedwa chifukwa chakuba. Nyumba zonse zinagwa. Mlongo wake Nana anabwerera kwawo ndipo anakwatiwa. Koma ndidzakumbukira Tenderetu nthawi zonse ndipo palibe amene angafufute Tenderetu m'moyo mwanga. “Ndimakusowa mnzanga Tenderetu. Ambuye asunge mzimu wako mu mtendere.”